Isaiah 24

Chilango cha Yehova pa Dziko Lapansi

1Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi
ndi kulisandutsa chipululu;
Iye adzasakaza maonekedwe ake
ndi kumwaza anthu ake onse.
2Aliyense zidzamuchitikira mofanana:
wansembe chimodzimodzi munthu wamba,
antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna,
antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi,
wogula chimodzimodzi wogulitsa,
wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa,
okongola chimodzimodzi okongoza.
3Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu
ndi kusakazikiratu.
Yehova wanena mawu awa.

4Dziko lapansi likulira ndipo likufota,
dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma,
anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
5Anthu ayipitsa dziko lapansi;
posamvera malangizo ake;
pophwanya mawu ake
ndi pangano lake lamuyaya.
6Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi;
anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo,
iwo asakazika
ndipo atsala ochepa okha.
7Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota;
onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
8Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha,
phokoso la anthu osangalala latha,
zeze wosangalatsa wati zii.
9Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo;
akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka;
nyumba iliyonse yatsekedwa.
11Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo;
chimwemwe chonse chatheratu,
palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12Mzinda wasanduka bwinja
zipata zake zagumuka.
13Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi
ndiponso pakati pa mitundu ya anthu.
Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa,
kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.

14Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe;
anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova;
ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda
“Wolungamayo.”

Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu!
Tsoka kwa ine!
Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo,
inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
17Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje
ndi msampha zikukudikirani.
18Aliyense wothawa phokoso la zoopsa
adzagwa mʼdzenje;
ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo
adzakodwa ndi msampha.

Zitseko zakumwamba zatsekulidwa,
ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
19Dziko lapansi lathyokathyoka,
ndipo lagawika pakati,
dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
20Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera
likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba;
lalemedwa ndi machimo ake.
Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.

21Tsiku limenelo Yehova adzalanga
amphamvu a kumwamba
ndiponso mafumu apansi pano.
22Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi
ngati amʼndende amene ali mʼdzenje.
Adzawatsekera mʼndende
ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
23Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi;
pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira;
pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu,
ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Copyright information for NyaCCL